Apolisi amanga wachiwiri kwa mtsogoleri wa chipani cha DPP mchigawo cha pakati a Alfred Gangata powaganizira mlandu wogwiritsa ntchito setifiketi ya fomu folo imene akuti adaipeza mwachinyengo.
Wofalitsa nkhani za apolisi mdziko muno a Peter Kalaya ati apolisi amanga a Gangata lero iwo atakadzipereka ku likulu la apolisi ku area 30 mu mzinda wa Lilongwe.
A Kalaya ati a Gangata akuganiziridwa kuti setifiketiyi imene adaipeza mchaka cha 2018 pa sukulu ya sekondale ya Chitowo m’boma la Dedza ndi ya chinyengo.