Mtsogoleri wa chipani cha Democtratic Progressive (DPP) a Professor Arthur Peter Mutharika alonjeza kuti chaka cha mawa akalowa m’boma azakonzanso zina mwa zinthu zomwe zasokonekela pansi pa ulamuliro wa a Lazarus Chakwera.
A Mutharika, omwenso ndi mtsogoleri wakale wa dziko lino, wanena izi pa mbuyo pa m’kumano omwe anali nawo ndi mafumu a m’boma la Machinga.
Malingana ndi a Mutharika, pa mkumanowu, mafumwa anadandaula kuti zinthu sizili bwino.
“Anandidandaulira...